11. Ana anga, musazengereza tsopano; popeza Yehova anakusankhani inu muime pamaso pace, kumtumikira Iye, ndi kuti mukhale atumiki ace ndi kufukiza zonunkhira.
12. Pamenepo ananyamuka Alevi, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoeli mwana wa Azariya, a ana a Akohati; ndi a ana a Merari, Kisi mwana wa Abidi, ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; ndi a Agerisoni, Yowa mwana wa Zima, ndi Edeni mwana wa Yowa;
13. ndi a ana a Elizafana, Simri ndi Yeueli; ndi a ana a Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
14. ndi a ana a Hemani, Yehudi ndi Simei ndi a ana a Yedutuni, Semaya ndi Uziyeli,