1 Mbiri 23:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atakalamba tsono Davide ndi kucuruka masiku, iye analonga mwana wace Solomo akhale mfumu ya Israyeli.

2. Ndipo anasonkhanitsa akuru onse a Israyeli, ndi ansembe ndi Alevi.

3. Ndipo anawerengedwa Alevi oyambira zaka makumi atatu ndi mphambu, ndipo ciwerengo cao kuwawerenga mmodzi mmodzi ndico amuna zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu.

4. A iwowa zikwi makumi awiri mphambu zinai anayang'anira nchito ya nyumba ya Yehova, ndi zikwi zisanu ndi cimodzi ndiwo akapitao ndi oweruza,

5. ndi zikwi zinai odikira; ndi zikwi zinai analemekeza Yehova ndi zoyimbira zimene ndinazipanga, anati Davide, kuti alemekeze nazo.

6. Ndipo Davide anawagawa magawo monga mwa ana a Levi: Gerisomu, Kohati, ndi Merari.

7. A Agerisomu: Ladani ndi Simeyi,

8. Ana a Ladani: wamkuru ndi Yehieli, ndi Zethamu, ndi Yoeli; atatu.

9. Ana a Simeyi: Selomoti, ndi Hazieli, ndi Hanani; atatu. Ndiwo akuru a nyumba za makolo a Ladani.

10. Ndi ana a Simeyi: Yahati, Zina, ndi Yeusi, ndi Beriya. Awa anai ndiwo ana a Simeyi.

11. Wamkuru wa iwo ndi Yahati, mnzace ndi Ziza; koma Yeusi ndi Beriya analibe ana ambiri, potero anakhala nyumba ya kholo yowerengedwa pamodzi.

12. Ana a Kohati: Amiramu, Izara, Hebroni, ndi Uzieli; anai.

13. Ana a Amiramu: Aroni, ndi Mose; ndipo Aroni anasankhidwa kuti apatule zopatulikitsa, iye ndi ana ace, kosalekeza, kufukiza pamaso pa Yehova, kumtumikira, ndi kudalitsa m'dzina lace kosatha.

1 Mbiri 23