1 Mbiri 21:14-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Momwemo Yehova anatumiza mliri pa Israyeli; ndipo adagwapo amuna zikwi makumi asanu ndi awiri a Israyeli.

15. Ndipo Mulungu anatuma mthenga ku Yerusalemu kuuononga; ndipo poti auononge, Yehova anapenya, naleka coipaci; nati kwa mthenga wakuononga, Cakwanira, bweza dzanja lako tsopano. Ndi mthenga wa Yehova anaima pa dwale la Orinani Myebusi,

16. Ndipo Davide anakweza maso ace, naona mthenga wa Yehova alikuima pakati pa dziko ndi thambo, ali nalo lupanga losolola m'dzanja lace, lotambasukira pa Yerusalemu. Pamenepo Davide ndi akuru obvala ziguduli anagwa nkhope zao pansi.

17. Ndipo Davide anati kwa Mulungu, Si ndine nanga ndalamulira kuti awerenge anthu? Inde, ndine amene ndacimwa ndi kucita coipa ndithu; koma nkhosa izi zinacitanji? dzanja lanu, Yehova Mulungu wanga, Gnditsutse ine ndi nyumba ya atate wanga, koma Gsatsutse anthu anu ndi kuwacitira mliri.

18. Pamenepo mthenga wa Yehova anauza Gadi kuti anene ndi Davide, akwere Davideyo kuutsira Yehova guwa la nsembe pa dwale la Orinani Myebusi,

19. Ndipo Davide anakwera monga mwa mau a Gadi adawanena m'dzina la Yehova.

20. Poceuka Orinani anaona wamthengayo; ndi ana ace amuna anai anali naye anabisala. Koma Orinani analikupuntha tirigu.

21. Ndipo pofika Davide kwa Orinani, Orinaniyo anapenyetsa, naona Davide, naturuka kudwale, nawerama kwa Davide, nkhope yace pansi.

22. Davide tsono anati kwa Orinani, Ndipatse padwale pano kuti ndimangepo guwa la nsembe la Yehova; undipatse gi pa mtengo wace wonse, kuti mliri ulekeke pa anthu.

23. Ndipo Orinani anati kwa Davide, Mulitenge, ndi mbuye wanga mfumu icite comkomera m'maso mwace; taonani, ndikupatsani ng'ombe za nsembe zopsereza; ndi zipangizo zopunthira zikhale nkhuni, ndi tirigu wa nsembe yaufa; ndizipereka zonse.

24. Koma mfumu Davide anati kwa Orinani, lai, koma ndidzaligula pa mtengo wace wonse; pakuti sindidzatengera Yehova ciri cako, kapena kupereka nsembe yopsereza yopanda mtengo wace.

1 Mbiri 21