22. Benaya mwana wa Yehoyada, mwana wa ngwazi ya ku Kabzeeli, wocita zazikuru, anapha ana awiri a Ariyeli wa ku Moabu; anatsikanso, napha mkango m'kati mwa dzenje nyengo ya cipale cofewa.
23. Anaphanso M-aigupto munthu wamkuru, msinkhu wace mikono isanu, ndi m'dzanja la M-aigupto munali mkondo ngati mtanda woombera nsaru; ndipo anamtsikira ndi ndodo, nakwatula mkondo m'dzanja la M-aigupto, namupha ndi mkondo wace womwe.
24. Izi anazicita Benaya mwana wa Yehoyada, namveka dzina mwa atatu amphamvuwo.
25. Taonani, anali wa ulemu woposa makumi atatuwo, koma sanafikana atatu oyamba aja; ndipo Davide anamuika mkuru wa olindirira ace.
26. Ndipo amphamvuwo a magulu a nkhondo ndiwo Asaheli mbale wa Yoabu, Elanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
27. Samoti Mharori, Helezi Mpeloni,
28. Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekoi, Abiezeri wa ku Anatoti,
29. Sibekai Mhusati, liai M-ahohi,
30. Maharai Mnetofati, Heledi mwana wa Bana Mnetofati,
31. Itai mwana wa Ribai wa Gibeya wa ana a Benjamini, Benaya Mpiratoni,
32. Horai wa ku mitsinje ya Gaasi, Abiyeli M-ariba,
33. Azmaveti Mbaharumi, Eliaba Mshaliboni;
34. ana a Hasemu Mgizoni; Yonatani mwana wa Sage Mharari,
35. Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,