1. Ndipo Benihadadi mfumu ya Aramu anamemeza khamu lace lonse la nkhondo; ndi mafumu makumi atatu mphambu awiri anali naye, pamodzi ndi akavalo ndi magareta; nakamangira Samaria misasa, naponyana nao nkhondo.
2. Natumiza mithenga lrumudzi kwa Ahabu mfumu ya Israyeli, nati kwa iye,