Zekariya 11:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Atero Yehova Mulungu wanga: Dyetsani zoweta zakukaphedwa;

5. zimene eni ace azipha, nadziyesera osaparamula; ndi iwo akuwagulitsa akuti, Alemekezedwe Yehova, pakuti ine ndine wolemera; ndi abusa ao sazicitira cifundo.

6. Pakuti sindidzacitiranso cifundo okhala m'dzikomo, ati Yehova; koma taonani, ndidzapereka anthu, yense m'dzanja la mnansi wace, ndi m'dzanja la mfumu yace; ndipo iwo adzakantha dzikoli, ndi m'dzanja mwao sindidzawalanditsa.

7. M'mwemo ndinadyetsa zoweta zakukaphedwa, ndizo zoweta zonyankhalala. Ndipo ndinadzitengera ndodo ziwiri; yina ndinaicha Cisomo, inzace ndinaicha Comanganitsa; ndipo ndinadyetsa zowetazo.

8. Ndipo ndinatha abusa atatuwo mwezi umodzi; pakuti mtima wanga unalema nao, ndi mtima waonso unaipidwa nane.

9. Pamenepo ndinati, Sindidzadyetsanso inu; cirikufa cife; cosoweka cisoweke; ndi zotsala zidyane, conse nyama ya cinzace.

10. Ndipo ndinatenga ndodo yanga Cisomo, ndi kuidula pakati, kuti ndiphwanye pangano langa ndinalicita ndi mitundu yonse ya anthu.

Zekariya 11