Yoswa 6:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma ku Yeriko anatseka pazipata, natsekedwa cifukwa ca ana a Israyeli, panalibe woturuka, panalibenso wolowa.

2. Ndipo Yehova ananena kwa Yoswa, Taona, ndapereka m'dzanja lako Yeriko ndi mfumu yace, ndi ngwazi zace.

3. Ndipo muzizungulira mudzi Inu nonse ankhondo, kuuzungulira mudzi kamodzi. Muzitero masiku asanu ndi limodzi.

4. Ndipo ansembe asanu ndi awiri azinyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga: za nkhosa zamphongo, natsogolere nazo likasa; koma tsiku lacisanu ndi ciwiri muzizungulira mudziwo kasanu ndi kawirio ndi ansembe aziliza mphalasazo.

Yoswa 6