Yoswa 4:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, utatha kuoloka Yordano mtundu wonse, Yehova ananena ndi Yoswa, nati,

2. Mudzitengere mwa anthu, amuna khumi ndi awiri, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

3. ndipo muwalamulire iwo ndi kuti, Mudzitengere pano pakati pa Yordano, poimapo mapazi a ansembe, miyala khumi ndi iwiri, ndi kuoloka nayo, ndi kulika m'mogona m'mene mugonamo usiku uno.

4. Pamenepo Yoswa anaitana amuna khumi ndi awiriwo amene anawaikiratu mwa ana a Israyeli, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

Yoswa 4