Yesaya 66:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atero Yehova, Kumwamba ndi mpando wanga wacifumu, ndi dziko lapansi ndi coikapo mapazi anga; mudzandimangira Ine nyumba yotani? ndi malo ondiyenera kupumamo ali kuti?

2. Pakuti zonsezi mkono wanga wazilenga, momwemo zonsezi zinaoneka, ati Yehova; koma ndidzayang'anira munthu uyu amene ali waumphawi, ndi wa mzimu wosweka, nanthunthumira ndi mau anga.

3. Wakupha ng'ombe alingana ndi wakupha munthu; iye wapereka nsembe ya mwana wa nkhosa alingana ndi wotyola khosi la garu; wothira nsembe yaufa akunga wothira mwazi wa nkhumba; wofukiza conunkhira akunga wodalitsa fano; inde iwo asankha njira zao zao, ndipo moyo wao ukondwerera m'zonyansa zao;

Yesaya 66