1. Atero Yehova, Sungani inu ciweruziro, ndi kucita cilungamo; pakuti cipulumutso canga ciri pafupi kudza, ndi cilungamo canga ciri pafupi kuti cib zumbulutsidwe,
2. Wodala munthu amene acita ici, ndi mwana wa munthu amene agwira zolimba ici, amene asunga sabata osaliipitsa, nasunga dzanja lace osacita nalo coipa ciri conse.
3. Mlendo amene wadziphatika yekha kwa Yehova asanene, kuti, Yehova adzandilekanitsa ndithu ndi anthu ace; pena mfule asanene, Taonani ine ndiri mtengo wouma.