Yesaya 52:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Kondwani zolimba, yimbani pamodzi, inu malo abwinja a pa Yerusalemu; pakuti Yehova watonthoza mtima wa anthu ace, waombola Yerusalemu.

10. Yehova wabvula mkono wace woyera pamaso pa amitundu onse; ndi malekezero onse a dziko lapansi adzaona cipulumutso ca Mulungu wathu.

11. Cokani inu, cokani inu, turukani ku Babulo; musakhudze kanthu kodetsa; turukani pakati pace, khalani okonzeka, inu amene munyamula zotengera za Yehova.

12. Pakuti simudzacoka mofulumira, kapena kunka mothawa; pakuti Yehova adzakutsogolerani, ndi Mulungu wa Israyeli adzadikira pambuyo panu.

13. Taonani, Mtumiki wanga adzacita mwanzeru; adzakwezedwa ndi kutukulidwa pamwamba, nadzakhala pamwambamwamba.

14. Monga ambiri anazizwa ndi iwe Israyeli, momwemo nkhope yace yaipitsidwa ndithu, kupambana munthu ali yense, ndi maonekedwe ace kupambana ana a anthu;

Yesaya 52