4. ndipo iwo adzaphuka pakati pa maudzu, ngati msondodzi m'mphepete mwa madzi.
5. Wina adzati, Ine ndiri wa Yehova; ndi wina adzadzicha yekha ndi dzina la Yakobo, ndipo wina adzalemba ndi dzanja lace, Ndine wa Yehova, ndi kudzicha yekha ndi mfunda wa lsrayeli.
6. Atero Yehova, Mfumu ya Israyeli ndi Mombolo wace, Yehova wa makamu, Ine ndiri woyamba ndi womariza, ndi popanda Ine palibenso Mulungu.
7. Ndipo ndani adzaitana monga Ine, ndi kulalikira ici ndi kundilongosolera ici, cikhazikitsire Ine anthu akale? milunguyo iwadziwitse zomwe zirinkudza, ndi za m'tsogolo.