9. Taona, zinthu zakale zaoneka, ndipo zatsopano Ine ndizichula; zisanabuke ndidzakumvetsani.
10. Yimbirani Yehova nyimbo yatsopano, ndi matamando ace kucokera ku malekezero a dziko lapansi; inu amene mutsikira kunyanja, ndi zonse ziri m'menemo, zisumbu ndi okhala mommo.
11. Cipululu ndi midzi yace ikweze mau ao, midzi imene Kedara akhalamo; okhala m'Sela ayimbe, akuwe kucokera pamwamba pa mapiri.
12. Apereke ulemerero kwa Yehova, anene matamando ace m'zisumbu.
13. Yehova adzaturuka ngati munthu wamphamvu; adzautsa nsanje ngati munthu wa nkhondo; Iye adzapfuula, inde adzakuwa zolimba; adzacita zamphamvu pa adani ace.
14. Ndakhala nthawi yambiri wosalankhula; ndakhala cete ndi kudzithungata ndekha; tsopano ndidzapfuula ngati mkazi wobala; ndidzapuma modukizadukiza ndi wefuwefu pamodzi.
15. Ndidzapasula mapiri ndi zitunda, ndi kuumitsa zitsamba zao zonse; ndi kusandutsa nyanja zisumbu, ndi kuumitsa matamanda.
16. Ndipo ndidzayendetsa akhungu m'khwalala, limene iwo salidziwa; m'njira zimene iwo sazidziwa ndidzawatsogolera; ndidzawalitsa mdima m'tsogolo mwao, ndi kulungamitsa malo okhota. Zinthu Izi ine ndidzacita, ndipo sindidzawasiya.