Yesaya 34:2-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti Yehova akwiyira amitundu onse, nacitira ukali khamu lao lonse; Iye wawaononga psiti, wawapereka kukaphedwa,

3. Ophedwa aonso adzatayidwa kunja, ndipo kununkha kwa mitembo yao kudzamveka, ndipo mapiri adzasungunuka ndi mwazi wao.

4. Ndipo makamu onse a kumwamba adzasungunuka, ndi miyamba idzapindika pamodzi ngati mpukutu; makamu ao onse adzafota monga tsamba limafota pampesa ndi kugwa, ndi monga tsamba lifota pamkuyu.

Yesaya 34