Yesaya 25:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga, ndidzakukuzani Inu, ndidzatamanda dzina lanu, cifukwa mwacita zinthu zodabwitsa, ngakhale: zauphungu zakale, mokhulupirika ndi m'zoonadi.

2. Cifukwa Inu mwasandutsa mudzi muunda; mudzi walinga bwinja; nyumba ya alendo kuti isakhale mudzi; sudzamangidwa konse.

3. Cifukwa cace anthu amphamvu adzakulemekezani Inu, mudzi wa mitundu yakuopsya udzakuopani Inu.

Yesaya 25