Yesaya 14:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Wagwadi kucokera kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mbanda kuca! Wagwetsedwa pansi, iwe wolefula amitundu!

13. Ndipo iwe unati mumtima mwako, Ndidzakwera kumwamba, ndidzakweza mpando wanga wacifumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pamwamba pa phiri la khamu, m'malekezero a kumpoto;

14. ndidzakwera pamwamba pa mitambo, ndidzafanana ndi Wam'mwambamwamba.

15. Koma udzatsitsidwa kunsi ku manda, ku malekezero a dzenje.

16. Iwo amene akuona iwe adzayang'anitsitsa iwe, nadzalingalira za iwe, ndi kuti, Kodi uyu ndi munthu amene ananthunthumiritsa dziko lapansi, amene anagwedeza maufumu;

Yesaya 14