23. Za Damasiko. Hamati ndi Aripadi ali ndi manyazi, cifukwa anamva malodza, asungunuka kunyanja, adera nkhawa osatha kukhala cete.
24. Damasiko walefuka, atembenukira kuti athawe, kunthunthumira kwamgwira; zobvuta ndi kulira zamgwira iye, ngati mkazi alimkudwala.
25. Alekeranji kusiya mudzi wa cilemekezo, mudzi wa cikondwero canga?
26. Cifukwa cace anyamata ace adzagwa m'miseu yace, ndipo anthu onse a nkhondo adzatontholetsedwa tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu.
27. Ndipo Ine ndidzayatsa moto m'khoma la Damasiko, udzathetsa zinyumba za Beni-Hadadi.