1. Ndipo Pasuri mwana wace wa Imeri wansembe, amene anali kapitao wamkuru m'nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya alikunenera zimenezi.
2. Ndipo Pasuri anampanda Yeremiya mneneriyo, namuika matangadza amene anali m'cipata ca kumtunda ca Benjamini, cimene cinali ku nyumba ya Yehova.
3. Ndipo panali m'mawa mwace, kuti Pasuri anaturutsa Yeremiya m'matangadzamo. Ndipo Yeremiya anati kwa iye, Yehova sanacha dzina lako Pasuri, koma Magorimisabibu.