Rute 2:11-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Boazi anayankha nanena naye, Anandifotokozera bwino zonse unacitira mpongozi wako atafa mwamuna wako; ndi kuti wasiya atate wako ndi mako, ndi dziko lobadwirako iwe, ndi kudza kwa anthu osawadziwa iwe kale.

12. Yehova akubwezere nchito yako, nakupatse mphotho yokwanira Yehova, Mulungu wa Israyeli, amene unadza kuthawira pansi pa mapiko ace.

13. Nati iye, Mundikomere mtima mbuye wanga, popeza mwandisangalatsa, popezanso mwanena cokondweretsa mtima wa mdzakazi wanu, ndingakhale ine sindine ngati mmodzi wa adzakazi anu.

Rute 2