Oweruza 19:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pamenepo anamlonga m'nyumba yace, napatsa aburu cakudya; ndipo iwo anasamba mapazi ao, nadya, namwa.

22. Pokondweretsa iwo mitima yao, taonani amuna a m'mudziwo, ndiwo anthu otama zopanda pace, anazinga nyumba, nagogodagogoda pacitseko; nati kwa mwini nyumba nkhalambayo ndi kuti, Turutsa mwamunayo adalowa m'nyumba mwako kuti timdziwe.

23. Ndipo munthu mwini nyumba anawaturukira nanena nao, lai, abale anga, musacite coipa cotere; popeza mwamuna uyu walowa m'nyumba mwanga, musacite copusa ici.

24. Taonani, mwana wanga wamkazi ndiye namwali, ndi mkazi wace wamng'onoyo siwa; ndiwaturutse iwo, muwacepetse iwo, ndi kuwacitira monga muyesa cokoma; koma mwamuna uyu musamcitire copusa ici.

25. Koma amunawo sanafuna kumvera; motero munthuyu anagwira mkazi wace wamng'ono, naturuka naye kwa iwo kunja; namdziwa iwo, nacita naye zoipa usiku wonse mpaka m'mawa; namlola acoke mbandakuca.

26. Nadza mkaziyo kutaca, nagwa pakhomo pa nyumba ya munthu padali mbuye wace, kufikira kutayera.

Oweruza 19