Oweruza 19:16-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo taonani, munthu nkhalamba anacokera ku nchito yace kumunda madzulo; munthuyu ndiye wa ku mapiri a Efraimu, nagonera ku Gibeya; kuma anthu pamenepo ndiwo Abenjamini.

17. Pamene anakweza maso ace anaona munthu wa pa ulendoyo m'khwalala la mudzi; ndi nkhalambayo inati, Umuka kuti? ufumira kuti?

18. Ndipo ananena nayo, Tirikucokera ku BetelehemuYuda, kumka ku mbali za mapiri a Efraimu, ndiko ndifumira ine; koma ndidamuka ku Betelehemu-Yuda; ndipo tsopano ndiri kumuka ku nyumba ya Yehova; koma palibe munthu wondipatsa nyumba.

19. Ngakhale maudzu ndi cakudya ca aburu athu ziriko; ndi mkate ndi vinyo zirikonso kwa ine ndi kwa mdzakazi wako ndi kwa mnyamata wokhala ndi aka polo ako; kosasowa kanthu.

20. Ndipo nkhalambayo inati, Mtendere ukhale ndi iwe, komatu, zosowa zako zonse ndidzakuparsa ndi ine; pokhapo usa gone m'khwalala.

21. Pamenepo anamlonga m'nyumba yace, napatsa aburu cakudya; ndipo iwo anasamba mapazi ao, nadya, namwa.

22. Pokondweretsa iwo mitima yao, taonani amuna a m'mudziwo, ndiwo anthu otama zopanda pace, anazinga nyumba, nagogodagogoda pacitseko; nati kwa mwini nyumba nkhalambayo ndi kuti, Turutsa mwamunayo adalowa m'nyumba mwako kuti timdziwe.

23. Ndipo munthu mwini nyumba anawaturukira nanena nao, lai, abale anga, musacite coipa cotere; popeza mwamuna uyu walowa m'nyumba mwanga, musacite copusa ici.

24. Taonani, mwana wanga wamkazi ndiye namwali, ndi mkazi wace wamng'onoyo siwa; ndiwaturutse iwo, muwacepetse iwo, ndi kuwacitira monga muyesa cokoma; koma mwamuna uyu musamcitire copusa ici.

25. Koma amunawo sanafuna kumvera; motero munthuyu anagwira mkazi wace wamng'ono, naturuka naye kwa iwo kunja; namdziwa iwo, nacita naye zoipa usiku wonse mpaka m'mawa; namlola acoke mbandakuca.

26. Nadza mkaziyo kutaca, nagwa pakhomo pa nyumba ya munthu padali mbuye wace, kufikira kutayera.

27. Pamene mbuye wace anauka mamawa, natsegula pakhomo pa nyumba, naturuka kumka ulendo wace, taona, mkazi wace wamng'onoyo, atagwa pakhomo pa nyumba ndi manja ace paciundo.

Oweruza 19