Oweruza 18:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pamenepo amuna asanuwa anacoka, nafika ku Laisi; naona anthu anali m'mwemo, kuti anakhalaokhazikika mtima, monga anakhala Asidoni, odekha ndi osatekeseka; popeza m'dzikomo munalibe mwini bwalo wakudtitsa manyazi m'cinthu ciri conse; nasiyana kutali ndi Asidoni, ndipo analibe kanthu ndi munthu ali yense.

8. Ndipo asanuwo anafikanso kwa abale ao ku Zora ndi Esitaoli; ndi abale ao ananena nao, Mutani inu?

9. Nati iwo, Taukani, tiwakwerere; pakuti tapenya dziko, ndipo taonani, ndilo lokoma ndithu; ndi inu muli cete kodi? musamacita ulesi kumuka ndi kulowa kulandira dzikolo,

10. Pomuka inu mudzafikira anthu okhazikika mtima ndi dziko ladtando; pakuti Mulungu walipereka m'dzanja lanu; pamenepo mposasowa kanthu kali konse kali pa dziko lapansi.

11. Pamenepo amuna mazana asanu ndi limodzi, omangira zida za nkhondo m'cuuno, anaphumulako a banja la a Dani, anacokera ku Zora, ndi ku Esitaoli.

Oweruza 18