Oweruza 16:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pamenepo anamgonetsa pa mabondo ace, naitana munthu, nameta njombi zace zisanu ndi ziwiri; nayamba kumzunza, nimcokera mphamvu yaceo

20. Ndipo anati, Afilisti akugwera, Samsoni. Nagalamuka iye m'tulo tace, nati, Ndizituruka ngati nthawi zina, ndi kudzitakasika. Koma sanadziwa kuti Yehova adamcokera.

21. Pamenepo Afilisti anamgwira, namkolowola maso, natsika naye ku Gaza, nammanga ndi maunyolo amkuwa; namperetsa m'kaidi.

22. Koma atammeta tsitsi la pamutu pace linayamba kumeranso.

23. Ndipo anasonkhana akalonga a Afilisti kuperekera Dagoni mulungu wao nsembe yaikuru, ndi kusekerera; pakuti anati, Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu m'dzanja lathu.

24. Ndipo pakumuona anthu analemekeza mulungu wao, pakuti anati, Mulungu wathu wapereka m'dzanja lathu mdani wathu, ndiye wakupasula dziko lathu, amene anatiphera ambiri.

Oweruza 16