11. M'milomo yako, mkwatibwi, mukukha uci,Uci ndi mkaka ziri pansi pa lilime lako;Kununkhira kwa zobvala zako ndi kunga kununkhira kwa Lebano,
12. Mlongwanga, mkwatibwi ndiye munda wotsekedwa;Ngati kasupe wotsekedwa, ndi citsime copikiza.
13. Mphukira zako ndi munda wamakangaza,Ndi zipatso zofunika, bonongwe ndi mphoka,
14. Mphoka ndi cikasu,Nzimbe ndi ngaho, ndi mitengo yonse yamtanthanyerere;Nipa ndi khonje, ndi zonunkhiritsa zonse zomveka.
15. Ndiwe kasupe wa m'minda,Citsime ca madzi amoyo,Ndi mitsinje yoyenda yocokera ku Lebano.