Nyimbo 4:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. M'milomo yako, mkwatibwi, mukukha uci,Uci ndi mkaka ziri pansi pa lilime lako;Kununkhira kwa zobvala zako ndi kunga kununkhira kwa Lebano,

12. Mlongwanga, mkwatibwi ndiye munda wotsekedwa;Ngati kasupe wotsekedwa, ndi citsime copikiza.

13. Mphukira zako ndi munda wamakangaza,Ndi zipatso zofunika, bonongwe ndi mphoka,

14. Mphoka ndi cikasu,Nzimbe ndi ngaho, ndi mitengo yonse yamtanthanyerere;Nipa ndi khonje, ndi zonunkhiritsa zonse zomveka.

15. Ndiwe kasupe wa m'minda,Citsime ca madzi amoyo,Ndi mitsinje yoyenda yocokera ku Lebano.

Nyimbo 4