Nyimbo 1:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Musayang'ane pa ine, pakuti ndada,Pakuti dzuwa landidetsa.Ana amuna a amai anandikwiyira,Anandisungitsa minda yamipesa;Koma munda wanga wanga wamipesa sindinausunga.

7. Ndiuze, iwe amene moyo wanga ukukonda,Umaweta kuti gulu lako?Umaligonetsa kuti pakati pa usana?Pakuti ndikhalirenji ngati wosoceraPambali pa magulu a anzako?

8. Ngati sudziwa, mkaziwe woposa kukongola,Dzituruka kukalondola bande la gululo,Nukawete ana a mbuzi zako pambali pa mahema a abusa.

9. Ndakulinganiza, wokondedwa wanga mnyamatawe,Ngati akavalo a magareta a Farao.

Nyimbo 1