Numeri 5:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Zopatulika za munthu ali yense ndi zace: ziti zonse munthu ali yense akapatsa wansembe, zasanduka zace.

11. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

12. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mkazi wa mwini akapatukira mwamuna wace, nakamcitira mosakhulupirika,

13. ndi munthu akagona naye, koma kumbisikira maso a mwamuna wace, ndikumng'unira; nadetsedwa mkaziyo, koma palibe mboni yomtsutsa, kapena sanamgwira alimkucita;

14. ndipo ukamgwira mwamuna mtima wansanje, kuti acitire nsanje mkazi wace, popeza wadetsedwa; kapena ukamgwira mtima wansanje, kuti amcitire mkazi wace nsanje angakhale sanadetsedwa;

Numeri 5