8. Ndipo asunge zipangizo zonse za cihema cokomanako, ndi udikiro wa ana a Israyeli, kuicita nchito ya kacisi.
9. Ndipo uzipereka Alevi kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna; apatsidwa kwa iye ndithu, ocokera kwa ana a Israyeli.
10. Koma uike Aroni ndi ana ace amuna, azisunga nchito yao ya nsembe; ndi mlendo wakusendera pafupi amuphe.
11. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
12. Ndipo taonani, Ine ndatenga Alevi kuwacotsa pakati pa ana a Israyeli m'malo mwa ana ovamba onse, oyamba kubadwa mwa ana a Israyeli; ndipo Aleviwo ndi anga.