Numeri 20:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Mose anasamula dzanja lace, napanda thanthwe kawiri ndi ndodo; ndipo madzi anaturukamo ocuruka, ndi khamulo linamwa, ndi zoweta zao zomwe.

12. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Popeza simunandikhulupirira Ine, kundipatula Ine pamaso pa ana a Israyeli, cifukwa cace simudzalowetsa msonkhano uwu m'dziko ndinawapatsali.

13. Awa ndi madzi a Meriba; popeza ana a Israyeli anatsutsana ndi Yehova, ndipo anapatulidwa mwa iwowa.

14. Pamenepo Mose anatumiza amithenga ocokera ku Kadesi kumuka kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Atero mbale wanu Israyeli, Mudziwa zowawa zonse zinatigwera;

Numeri 20