Mateyu 9:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Iye analowa m'ngalawa, naoloka, nadza kumudzi kwao.

2. Ndipo onani, anabwera naye kwa Iye munthu wamanjenje, wakugona pachika: ndipo Yesu pakuona cikhulupiriro cao, anati kwa wodwalayo, Limba mtima, mwana, macimo ako akhululukidwa.

3. Ndipo onani, ena a alembi ananena mumtima mwao, Uyu acitira Mulungu mwano.

4. Ndipo Yesu, pozindikira maganizo ao, anati, Cifukwa canji mulinkuganizira zoipam'mitimayanu?

5. pakuti capafupi nciti, kunena, Macimo ako akhululukidwa; kapena kunena, Tanyamuka nuyende?

Mateyu 9