Mateyu 5:32-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. koma Ine ndinena kwa inu, kuti 4 yense wakucotsa mkazi wace, kosati cifukwa ca cigololo, amcititsa cigololo: ndipo amene adzakwata wocotsedwayo acita cigololo.

33. Ndiponso, munamva kuti kunanenedwa kwa iwo akale, 5 Usalumbire konama, koma udzapereka kwa Ambuye zolumbira zako:

34. koma Ine ndinena kwa inu, 6 Musalumbire konse, kapena kuchula Kumwamba, cifukwa kuli cimpando ca Mulungu;

35. 7 kapena kuchula dziko lapansi, cifukwa liri popondapo mapazi ace; kapena kuchula Yerusalemu, cifukwa kuli mzinda wa Mfumu yaikurukuru.

36. 8 Kapena usalumbire ku mutu wako, cifukwa sungathe kuliyeretsa mbu kapena kulidetsa bii tsitsi limodzi.

37. 9 Kama manenedwe anu akhale, Inde, inde; Iai, iai; ndipo coonjezedwa pa izo cicokera kwa woipayo.

38. Munamva kuti kunanenedwa, 10 Diso kulipa diso, ndi dzino kulipa dzino:

39. koma ndinena kwa inu, 11 Musakanize munthu woipa; koma amene adzakupanda iwe pa tsaya lako Lamanja, umtembenuzire linanso.

40. Ndipo kwa iye wofuna kupita nawe kumlandu ndi kutenga malaya ako, umlolezenso copfunda cako.

41. Ndipo 12 amene akakukakamiza kumperekeza njira imodzi, upite naye ziwiri.

42. Kwa iye wopempha iwe umpatse, ndipo kwa iye 13 wofuna kukukongola usampotolokere.

43. Munamva kuti kunanenedwa, 14 Uzikondana ndi mnansi wako, ndi kumuda mdani wako:

44. koma Ine ndinena kwa inu, 15 Kondanani nao adani anu, ndi 16 kupempherera iwo akuzunza inu;

45. kotero kuti mukakhale ana a Atate wanu wa Kumwamba; cifukwa Iye amakwezera dzuwa lace pa oipa ndi pa abwino, namabvumbitsira mvula pa olungama ndi pa osalungama.

46. Cifukwa kuti 17 ngati muwakonda akukondana ndi inu mphotho yanji muli nayo? kodi angakhale amisonkho sacita comweco?

47. Ndipo ngati mulankhula abale anu okha okha, mucitanji coposa ena? Kodi angakhale anthu akunja sacita comweco?

48. Cifukwa cace inu 18 mukhale angwiro, monga Atate wanu wa Kumwamba ali wangwiro.

Mateyu 5