Mateyu 24:43-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Koma 4 dziwani ici, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yiti mbala ikudza, iye akadadikira, ndipo sakadalola kuti nyumba yace ibooledwe.

44. Cifukwa cace 5 khalani inunso okonzekeratu; cifukwa munthawi m'mene simuganizira, Mwana wa munthu adzadza.

45. 6 Ndani kodi ali kapolo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wace anamkhazika woyang'anira banja lace, kuwapatsa zakudya pa nthawi yace?

46. Wodala kapolo amene mbuye wace, pakufika, adzampeza iye alikucita cotero.

47. Indetu, ndinena kwa inu, kuti 7 adzamkhazika iye woyang'anira zinthu zace zonse.

48. Koma kapolo woipa akanena mumtima mwace, Mbuye wanga wacedwa;

49. nadzayamba kupanda akapolo anzace, nadya ndi kumwa pamodzi ndi oledzera;

50. mbuye wa kapoloyo adzafika tsiku losamuyembekeza iye, ndi nthawi yosadziwa iye,

51. nadzamdula, nadzaika pokhala pace ndi anthu onyenga; 8 pomwepo padzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mateyu 24