40. Pomwepo 2 adzakhala awiri m'munda; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa:
41. awiri adzakhala opera pamphero; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.
42. 3 Cifukwa cace dikirani, pakuti simudziwa tsiku lace lakufika Ambuye wanu.
43. Koma 4 dziwani ici, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yiti mbala ikudza, iye akadadikira, ndipo sakadalola kuti nyumba yace ibooledwe.
44. Cifukwa cace 5 khalani inunso okonzekeratu; cifukwa munthawi m'mene simuganizira, Mwana wa munthu adzadza.
45. 6 Ndani kodi ali kapolo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wace anamkhazika woyang'anira banja lace, kuwapatsa zakudya pa nthawi yace?