Mateyu 24:40-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Pomwepo 2 adzakhala awiri m'munda; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa:

41. awiri adzakhala opera pamphero; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

42. 3 Cifukwa cace dikirani, pakuti simudziwa tsiku lace lakufika Ambuye wanu.

43. Koma 4 dziwani ici, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yiti mbala ikudza, iye akadadikira, ndipo sakadalola kuti nyumba yace ibooledwe.

44. Cifukwa cace 5 khalani inunso okonzekeratu; cifukwa munthawi m'mene simuganizira, Mwana wa munthu adzadza.

45. 6 Ndani kodi ali kapolo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wace anamkhazika woyang'anira banja lace, kuwapatsa zakudya pa nthawi yace?

Mateyu 24