Mateyu 24:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. cifukwa Akristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikuru ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

25. Cifukwa cace akanena kwa inu, Onani, Iye ali m'cipululu; musamukeko.

26. Onani, ali m'zipinda; musabvomereze.

27. Pakuti monga mphezi idzera kum'mawa, nionekera kufikira kumadzulo; kotero kudzakhalanso kufika kwace kwa Mwana wa munthu.

28. Kumene kuli konse uli mtembo, miimba Idzasonkhanira konko.

29. Koma pomwepo, atapita masauko a masiku awo, dzuwa lidzadetsedwa, ndi mwezi sudzaonetsa kuwala kwace, ndi nyenyezi zidzagwa kucokera kumwamba, ndi mphamvu za kumwamba zidzagwedezeka:

Mateyu 24