Mateyu 23:24-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Atsogoleri akhungu inu, akukuntha udzudzu, koma ngamila mummeza.

25. Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mutsuka kunja kwace kwa cikho ndi mbale, koma m'katimo iwo adzala ndi kulanda ndi kusadziletsa.

26. Mfarisi iwe wakhungu, yambotsuka m'kati mwa cikho ndi mbale, kuti kunja kwace kukhalenso koyera.

27. Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mufanafana ndi manda opaka njereza, amene aonekera okoma kunja kwace, koma adzala m'katimo ndi mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zonse.

28. Comweco inunso muonekera olungama pamaso pa anthu, koma m'kati muli odzala ndi cinyengo ndi kusayeruzika.

29. Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mumanga nyumba za pa manda a aneneri, ndipo mukonza manda a anthu olungama,

30. ndi kuti, Ife tikadakhala m'masiku a makolo anthu, sitikadakhala oyanjana nao pa mwazi wa aneneri.

31. Pomwepo mutsimikiza nokha, kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.

32. Dzazani inu muyeso wa makolo anu.

33. Njoka inu, obadwa inu a mamba, mudzatha bwanji kuthawa kulanga kwace kwa gehena?

34. Cifukwa ca ici, onani, ndituma kwa inu aneneri ndi anzeru ndi alembi; ena a iwo mudzawapha, mudzawapacika; ndi ena a iwo mudzawakwapula m'masunagoge mwanu, ndi kuwazunza, kucokera ku mudzi umodzi, kufikira ku mudzi wina;

Mateyu 23