Mateyu 23:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pomwepo Yesu analankhula ndi makamu a anthu ndi ophunzira ace,

2. nanena, Alembi ndi Afarisi akhala pa mpando wa Mose;

3. cifukwa cace zinthu ziri zonse zimene iwo akauza inu, citani nimusunge; koma musatsanza nchito zao; pakuti iwo amalankhula, komasamacita.

4. Inde, amanga akatundu olemera ndi osautsa ponyamula, nawasenza pa mapewa a anthu; koma iwo eni okha safuna kuwasuntha amenewo ndi cala cao.

5. Koma amacita nchito zao zonse kuti aonekere kwa anthu; pakuti akulitsa citando cace ca njirisi zao, nakulitsa mphonje,

6. nakonda malo a ulemu pamapwando, ndi mipando ya ulemu m'masunagoge,

7. ndi kulankhulidwa m'misika, ndi kuchedwa ndi anthu, Rabi.

8. Koma inu musachedwa Rabi; pakuti Mphunzitsi wanu ali mmodzi, ndipo inu nonse muli abale.

9. Ndipo inu musachule wina atate wanu pansi pano, pakuti alipo mmodzi ndiye Atate wanu wa Kumwamba.

10. Ndipo musachedwa atsogoleri, pakuti alipo mmodzi Mtsogoleri wanu, ndiye Kristu.

11. Koma wamkuru wopambana wa inu adzakhala mtumiki wanu.

Mateyu 23