Mateyu 2:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo iwe: Betelehemu, dziko la Yudeya,Sukhala konse wamng'onong'ono mwa akuru a Yudeya.Pakuti Wotsogolera adzacokera mwaiwe,Amene adzaweta anthu anga Aisrayeli.

7. Pomwepo Herode anawaitana Anzeruwo m'tseri, nafunsitsa iwo nthawi yace idaoneka nyenyeziyo.

8. Nawatumiza ku Betelehemu, nati, Yendani mufunitsitse za kamwanako; ndipo pamene mudzampeza, mundibwezere mau, kuti inenso ndidzadze kudzamlambira Iye.

9. Ndipo iwo, m'mene anamva mfumu, anamuka; ndipo onani, nyenyezi ija anaiona kum'mawa, inawatsogolera iwo, kufikira inadza niima pamwamba pomwe panali kamwanako.

10. Ndipo iwo poona nyenyeziyo, anakondwera ndi kukondwera kwakukuru.

Mateyu 2