Mateyu 13:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. koma m'mene anthu analinkugona, mdani wace anadza, nafesa namsongole pakati pa tirigu, nacokapo.

26. Koma pamene mmera unakula, nubala cipatso, pomwepo anaonekeranso namsongole.

27. Ndipo anyamata ace a mwini nyumbayo anadza, nati kwa iye, Mbuye, kodi simunafesa mbeu zabwino m'munda mwanu? nanga wacokera kuti namsongoleyo?

28. Ndipo iye ananena kwa iwo, Munthu mdani wanga wacicita ici. Ndipo anyamata anati kwa iye, Kodi mufuna tsopano kuti timuke, tikamsonkhanitse uyo pamodzi?

29. Koma iye anati, lai, kuti kapena m'mene mukasonkhanitsa namsongoleyo, mungazulenso tirigu pamodzi naye.

Mateyu 13