Mateyu 10:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. pakuti wolankhula si ndinu, koma Mzimu wa Atate wanu akulankhula mwa inu.

21. Ndipo mbale adzapereka mbale wace kuimfa, ndi atate mwana wace: ndipo ana adzatsutsa akuwabala, nadzawafetsa iwo.

22. Ndipo adzada inu anthu onse cifukwa ca dzina langa; koma iye wakupirira kufikira cimariziro, iyeyu adzapulumutsidwa.

23. Koma pamene angakuzunzeni inu m'mudzi uwu, thawirani mwina: indetu ndinena kwa inu, Simudzaitha mizinda ya Israyeli, kufikira Mwana wa munthu atadza.

24. Wophunzira saposa mphunzitsi wace, kapena kapolo saposa mbuye wace.

Mateyu 10