Masalmo 22:4-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Makolo athu anakhulupirira Inu:Anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.

5. Anapfuula kwa Inu, napulumutsidwa:Anakhulupita Inu, ndipo sanacita manyazi.

6. Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai:Cotonza ca anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.

7. Onse akundipenya andiseka:Akwenzula, apukusa mutu, nati,

8. Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa,Amlanditse tsopano popeza akondwera naye.

9. Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa:Wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.

10. Cibadwire ine anandisiyira Inu:Kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.

11. Musandikhalire kutali; pakuti nsautso iri pafupi:Pakuti palibe mthandizi.

12. Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga:Mphongo zolimba za ku Basana zandizungulira,

13. Andiyasamira m'kamwa mwao,Ngati mkango wozomola ndi wobangula.

14. Ndathiridwa pansi monga madzi,Ndipo mafupa anga onse anaguluka:Mtima wanga ukunga sera; Wasungunuka m'kati mwa matumbo anga,

Masalmo 22