Masalmo 102:17-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,Osapepula pemphero lao.

18. Ici adzacilembera mbadwo ukudza;Ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19. Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ace opatulika;Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20. Kuti amve kubuula kwa wandende;Namasule ana a imfa,

21. Kuti anthu alalikire dzina la Yehova m'Ziyoni,Ndi cilemekezo cace m'Yerusalemu;

22. Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,Ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23. Iye analanda mphamvu yanga panjira;Anacepsa masiku anga.

Masalmo 102