6. Koma Yesu anati, Mlekeni, mumbvutiranji? wandicitira Ine nchito yabwino.
7. Pakuti muli nao aumphawi pamodzi ndi inu masiku onse, ndipo pali ponse pamene mukafuna mukhoza kuwacitira zabwino; koma Ine simuli nane masiku onse.
8. Iye wacita cimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m'manda.
9. Ndipo ndithu ndinena ndi inu, Ponse pamene padzalalikidwa Uthenga Wabwino ku dziko lonse lapansi, icinso cimene anacita mkazi uyu cidzanenedwa, cikhale comkumbukira naco.