Marko 14:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma Yesu anati, Mlekeni, mumbvutiranji? wandicitira Ine nchito yabwino.

7. Pakuti muli nao aumphawi pamodzi ndi inu masiku onse, ndipo pali ponse pamene mukafuna mukhoza kuwacitira zabwino; koma Ine simuli nane masiku onse.

8. Iye wacita cimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m'manda.

9. Ndipo ndithu ndinena ndi inu, Ponse pamene padzalalikidwa Uthenga Wabwino ku dziko lonse lapansi, icinso cimene anacita mkazi uyu cidzanenedwa, cikhale comkumbukira naco.

Marko 14