Macitidwe 2:38-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Koma Petro anati kwa iwo, Lapani, batizidwani yense wa inu m'dzina la Yesu Kristu kuloza ku cikhululukiro ca macimo anu; ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.

39. Pakuti lonjezano 1 liri kwa inu, ndi kwa ana anu, 2 ndi kwa onse akutali, 3 onse amene Ambuye Mulungu wathu adzaitana.

40. Ndipo ndi mau ena ambiri anacita umboni, nawadandaulira iwo, nanena, Mudzipulumutse kwa mbadwo uno wokhotakhota.

41. Pamenepo iwo amene analandira mau ace anabatizidwa; ndipo anaonjezedwa tsiku lomwelo anthu ngati zikwi zitatu.

42. Ndipo 4 anali cikhalire m'ciphunzitso ca atumwi ndi m'ciyanjano, m'kunyema mkate ndi mapemphero.

Macitidwe 2