37. Ndipo palibe munthu atsanulira vinyo watsopano m'matumba akale; cifukwa ngati atero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba, ndipo ameneyo adzatayika, ndi matumba adzaonongeka.
38. Koma kuyenera kutsanulira vinyo watsopano m'matumba atsopano.
39. Ndipo palibe munthu atamwa vinyo wakale afuna watsopano; pakuti anena, Wakale ali wokoma.