Luka 5:37-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Ndipo palibe munthu atsanulira vinyo watsopano m'matumba akale; cifukwa ngati atero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba, ndipo ameneyo adzatayika, ndi matumba adzaonongeka.

38. Koma kuyenera kutsanulira vinyo watsopano m'matumba atsopano.

39. Ndipo palibe munthu atamwa vinyo wakale afuna watsopano; pakuti anena, Wakale ali wokoma.

Luka 5