Levitiko 20:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. pamenepo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi banja lace, ndi kumsadza iye, ndi onse akumtsata ndi cigololo kukacita cigololo kwa Moleke, kuwacotsa pakati pa anthu a mtundu wao.

6. Ndipo munthu wakutembenukira kwa obwebweta ndi anyanga kuwatsata ndi cigololo, nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndipo ndidzamsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace.

7. Cifukwa cace dzipatuleni, nimukhale oyera; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

8. Ndipo musunge malemba anga ndi kuwacita; Ine ndine Yehova wakupatula inu.

Levitiko 20