Levitiko 20:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Mwamuna akagona ndi nyama amuphe ndithu; muiphenso nyamayi.

16. Mkazi akasendera kwa nyama iri yonse kugonana nayo, umuphe mkaziyo, ndi nyama yomwe; muwaphe ndithu; mwazi wao ukhale pamtu pao.

17. Munthu akatenga mlongo wace, mwana wamkazi wa atate wace, kapena mwana wamkazi wa mai wace, nakaona thupi lace, ndi mlongoyo akaona thupi lace; cocititsa manyazi ici; ndipo awasadze pamaso pa ana a anthu ao; anabvula mlongo wace; asenze mphulupulu yace.

18. Munthu akagona ndi mkazi ali mumsambo, nakambvula, anabvula kasupe wace, ndi iye mwini anabvula kasupe wa nthenda yace; awadule onse awiri pakati pa anthu a mtundu wao.

19. Usamabvula mbale wa mai wako, kapena mlongo wa atate wako; popeza anabvula abale ace; asenze mphulupulu yao.

20. Munthu akagona ndi mkazi wa mbale wa atate wace, nabvula mbale wa atate wace; asenze kucimwa kwao; adzafa osaona ana.

Levitiko 20