7. Onsewo atentha ngati ng'anjo, natha oweruza ao, agwa mafumu ao onse; palibe mmodzi mwa iwo wakuitana Ine.
8. Efraimu asokonezana nayo mitundu ya anthu; Efraimu ndiye kamtanda ka mkate kosatembenuzidwa.
9. Alendo anatha mphamvu yace osacidziwaiye; imvi zomwe zampakiza osacidziwa iye,
10. Ndipo kudzikuza kwa Israyeli kumcitira umboni pamaso pace; koma sanabwerera kumka kwa Yehova Mulungu wao, kapena kumfunafuna mwa ici conse.
11. Ndipo Efraimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Aigupto, amuka kwa Asuri.
12. Pamene amuka ndidzawayalira ukonde wanga, ndidzawagwetsa ngati mbalame za m'mlengalenga, ndidzawalanga monga udamva msonkhano wao.
13. Tsoka kwa iwowa! pakuti anandizembera; cionongeko kwa iwowa! pakuti anandilakwira; ndikadawalanditsa Ine, koma anandinenera zabodza.