20. Ndidzakutomeranso ukhale wanga mokhulupirika, ndipo udzadziwa Yehova.
21. Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, ndidzabvomereza, ati Yehova, ndidzabvomereza thambo, ndi ilo lidzabvomereza dziko lapansi;
22. ndi dziko lapansi lidzabvomereza tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta; ndi izi zidzabvomereza Yezreeli.
23. Ndipo ndidzadzibzalira iye m'nthaka, ndipo ndidzacitira cifundo Wosacitidwa-cifundo; ndipo ndidzati kwa Si-anthu-anga, Muli anthu anga; ndipo iwo adzati, Ndinu Mulungu wathu.