Genesis 37:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Tiyeni timgulitse iye kwa Aismayeli, tisasamulire iye manja; cifukwa ndiye mbale wathu, thupi lathu. Ndipo anamvera iye abale ace.

28. Ndipo ana pita pamenepo Amidyani a malonda: ndipo anamturutsa namkweza Yosefem'dzenjemo, namgulitsa kwa Aismayeli ndi ndalama zasiliva makumi awiri; ndipo ananka naye Yosefe ku Aigupto.

29. Ndipo Rubeni anabwera kudzenje, ndipo taonani, Yosefe mulibe m'dzenjemo: ndipo iye anang'amba nsaru yace.

30. Ndipo anabwera kwa abale ace, nati, Mwana palibe; ndipo ine ndipita kuti?

31. Ndipo anatenga malaya ace a Yosefe, napha tonde, nabvika malaya m'mwazi wace:

Genesis 37