Genesis 31:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. M'dzanja langa muli mphamvu yakucitira iwe zoipa koma Mulungu wa atate wako anati kwa ine usiku walero, kuti, Tadziyang'anira wekha, usanene kwa Yakobo kapena zabwino kapena zoipa.

30. Tsono ungakhale ukadamuka cifukwa mtima wako ulinkukhumba nyumba ya atate wako, bwanji waba iwe milungu yanga?

31. Ndipo anayankha Yakobo nati kwa Labani, Cifukwa ndinaopa: cifukwa kuti, ndinati, Kapena udzandilanda ine ana ako akazi.

32. Ali yense umpeza ali nayo milungu yako, asakhale ndi movo: pamaso pa abale athu, tayang'anira zako ziri ndi ine, nuzitenge wekha. Pakuti sanadziwe Yakobo kuti Rakele anaiba.

33. Ndipo Labani analowa m'hema wa Yakobo, ndi m'hema wa Leya, ndi m'mahema a adzakazi awiri aja; koma sanapeze, Ndipo anaturuka m'hema wa Leya nalowa m'hema wa Rakele.

34. Ndipo Rakele anatenga aterafiwo nabisa pa cokhalira ca ngamila, nakhala pamenepo, Ndipo Labani anafunafuna m'hema monse, koma sanawapeze.

Genesis 31