Genesis 13:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. cifukwa kuti dziko lonse limene ulinkuona, ndidzakupatsa iwe ndi mbeu yako nthawi yonse.

16. Ndipo ndidzayesa mbeu yako monga pfumbi lapansi: cotere kuti ngati munthu angathe kuwerenga pfumbi lapansi, comweconso mbeu yako idzawerengedwa.

17. Tauka, nuyendeyendc m'dzikoli m'litari mwace ndi m'mimba mwace; cifukwa kuti ndidzakupatsa iwe limenelo.

18. Ndipo Abramu anasuntha hema wace nafika nakhala pa mitengo yathundu ya pa Mamre, imene iri m'Hebroni, nammangira Yehova kumeneko guwa la nsembe.

Genesis 13